Psalms 124

Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
anene tsono Israeli,
2akanapanda kukhala mbali yathu Yehova,
potiwukira anthuwo,
3iwo atatipsera mtima,
akanatimeza amoyo;
4chigumula chikanatimiza,
mtsinje ukanatikokolola,
5madzi a mkokomo
akanatikokolola.

6Atamandike Yehova,
amene sanalole kuti tikhale chakudya cha mano awo.
7Moyo wathu wawonjoka ngati mbalame
yokodwa mu msampha wa mlenje;
msampha wathyoka,
ndipo ife tapulumuka.
8Thandizo lathu lili mʼdzina la Yehova
wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Copyright information for NyaCCL